Poyemnda Ndi Mbuye
[1]
Poyenda ndi Mbuye, mkuwala kwaceko, Aunikira m’njira mwathu;
Pakugwaira ntchito amakhala nafe, Ndi onse amene amvera.
CHORUS
Khulupira, palibenso njira, Yakukondwa mwa Yesu,
Komatu kumvera.
[2]
Mthunzi sungagwetu, pena mtambo mmwamba, Komatu azipirikitsa;
Nkhawa ndi cisoni zidzacoka ngati, Tikhulupira ndi kumvera.
[3]
Cifukwa ca ntchito ndi zisoni zathu, Mpaka titadziperekatu;
Cifukwa cifundo ndi cimwemwe cace, Amapatsa anthu omvera.
[4]
Pompo mciyanjano tidzakhala naye, Kapena kuyenda ndi Iye;
Ndipo tidzacita cifuniro cace, Tidzakhala omvera ndithu.
Support Mysongbooks
Support us by joining the Buy Me A Coffee community and making a small donation, you can help us expand our library and ensure that music lovers everywhere can enjoy their favorite songs to the fullest. We're passionate about music, and we know you are too, so let's work together to keep the music alive.
Thank you for being a part of our community and supporting our mission to provide the best lyrics library on the internet.