Patseni Bible
[1]
Patseni Bible ndilo ndikufuna, Ndi cotitsogolera njirayo;
Monga mapiri oonetsa kwathu, Obweza anthu osocerawo.
CHORUS:
Patseni Bible ndilo mau ace, Mau oyera a Mulunguyo,
Ndilo pangano la cikondi cace, ndi nyali mnjira yonka mwambambo.
[2]
Patseni Bible ndilo ndikufuna, Mmene usweka mtima wangawo
Patseni mau a Ambuye Yesu, Mau okondweretsa mmtimanga.
[3]
Patseni Bible ndilo ndikufuna, Nyali ya kusonyeza njirayo,
Mmene ndingagwe lindipulumutsa, Lindisonyeza tchimo langalo.
[4]
Patseni Bible ndilo ndikufuna, Liunikira a mu mdimawo,
Ndilo ciyembekezo kwa olira, Ndi nyali m’njira yonka mmwambamo.
Support Mysongbooks
Support us by joining the Buy Me A Coffee community and making a small donation, you can help us expand our library and ensure that music lovers everywhere can enjoy their favorite songs to the fullest. We're passionate about music, and we know you are too, so let's work together to keep the music alive.
Thank you for being a part of our community and supporting our mission to provide the best lyrics library on the internet.