Mlonda, Tandiuze Ine
[1]
Mlonda, tandiuze ine, Kunja kuli cutako?
Zosonyeza kudza kwace, Kodi zionekadi?
Inde, Mlendo, taonanil, Kuca kwayandikiratu,
Bvala za kukoma zako, Kuli kuca, dzuka ’we.
2. Mlonda, nyali iunika Mommo m’njira mwakomo;
Zozizwitsa m’dziko monse, Zisonyeza tsikulo.
Podzaomba pa lipenga, Pakudzuka a ku manda,
Omwalira mwa Ambuye, Adzabvala cosafa.
[3]
Mlonda, pfu’la liri kudza Tsiku lalikurulo.
Onse alalike kuti, Mfumu yayandkatu.
Inde, mlendo ’we, ndiona, Dziko lopambana lija.
Mzinda wopambana yonse, Uoneka tsidyalo.
[4]
Mlonda, undiuze ine, Za mu mzinda momwemo,
Mmene Mfumu ikukhala, Pa cimpando caceco.
Dziko lija likuwala Ndi ulemerero wace;
Kuli dzuwa ndi mitengo, Ndi mitsinje yoposa.
[5]
Dzuwa lituruka ndithu, La usana womwewo.
Onse alalike kuti, Tsiku layandikatu.
Aulendo aonenso, Kuli phiri la Mulungu;
Tidzafika, konko msanga, Tidzakondwererako
Support Mysongbooks
Support us by joining the Buy Me A Coffee community and making a small donation, you can help us expand our library and ensure that music lovers everywhere can enjoy their favorite songs to the fullest. We're passionate about music, and we know you are too, so let's work together to keep the music alive.
Thank you for being a part of our community and supporting our mission to provide the best lyrics library on the internet.